Salimo 53
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. 
 
1 Chitsiru chimati mu mtima mwake,  
“Kulibe Mulungu.”  
Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;  
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.   
   
 
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano  
pa ana a anthu  
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,  
wofunafuna Mulungu.   
3 Aliyense wabwerera,  
iwo onse pamodzi akhala oyipa;  
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,  
ngakhale mmodzi.   
   
 
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;  
anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,  
ndipo sapemphera kwa Mulungu?   
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu  
pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.  
Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;  
inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.   
   
 
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!  
Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,  
lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!