Salimo 52
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.” 
 
1 Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?  
Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,  
iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?   
2 Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;  
lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,  
ntchito yako nʼkunyenga.   
3 Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.  
Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.  
Sela
   
4 Umakonda mawu onse opweteka,  
iwe lilime lachinyengo!   
   
 
5 Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:  
iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;  
iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.   
6 Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;  
adzamuseka nʼkumanena kuti,   
7 “Pano tsopano pali munthu  
amene sanayese Mulungu linga lake,  
koma anakhulupirira chuma chake chambiri  
nalimbika kuchita zoyipa!”   
   
 
8 Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi  
wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;  
ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu  
kwa nthawi za nthawi.   
9 Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;  
chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera  
pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.