Salimo 14
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. 
 
1 Chitsiru chimati mu mtima mwake,  
“Kulibe Mulungu.”  
Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa;  
palibe amene amachita zabwino.   
   
 
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi,  
kuyangʼana anthu onse  
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,  
amene amafunafuna Mulungu.   
3 Onse atembenukira kumbali,  
onse pamodzi asanduka oyipa;  
palibe amene amachita zabwino,  
palibiretu ndi mmodzi yemwe.   
   
 
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse?  
Akudya anthu anga ngati chakudya chawo  
ndipo satamanda Yehova?   
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu,  
pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.   
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka,  
koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.   
   
 
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni!  
Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake,  
Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!