Salimo 129
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. 
 
1 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”  
anene tsono Israeli;   
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,  
koma sanandipambane.   
3 Anthu otipula analima pa msana panga  
ndipo anapangapo mizere yayitali:   
4 Koma Yehova ndi wolungama;  
Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”   
   
 
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni  
abwezedwe pambuyo mwamanyazi.   
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,  
umene umafota usanakule;   
7 sungadzaze manja a owumweta  
kapena manja a omanga mitolo.   
8 Odutsa pafupi asanene kuti,  
“Dalitso la Yehova lili pa inu;  
tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”