Salimo 128
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. 
 
1 Odala ndi onse amene amaopa Yehova,  
amene amayenda mʼnjira zake.   
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako;  
madalitso ndi chuma zidzakhala zako.   
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka  
mʼkati mwa nyumba yako;  
ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi  
kuzungulira tebulo lako.   
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa  
amene amaopa Yehova.   
   
 
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni  
masiku onse a moyo wako;  
uwone zokoma za Yerusalemu,   
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.  
   
 
Mtendere ukhale ndi Israeli.