Salimo 128
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
Odala ndi onse amene amaopa Yehova,
amene amayenda mʼnjira zake.
Udzadya chipatso cha ntchito yako;
madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka
mʼkati mwa nyumba yako;
ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi
kuzungulira tebulo lako.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa
amene amaopa Yehova.
 
Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni
masiku onse a moyo wako;
uwone zokoma za Yerusalemu,
ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.
 
Mtendere ukhale ndi Israeli.