Salimo 127
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. 
 
1 Yehova akapanda kumanga nyumba,  
omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe.  
Yehova akapanda kulondera mzinda,  
mlonda akanangolondera pachabe.   
2 Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa  
ndi kusagona msanga madzulo,  
kuvutikira chakudya choti mudye,  
pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.   
   
 
3 Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova,  
ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.   
4 Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja  
mwa munthu wankhondo.   
5 Wodala munthu  
amene motengera mivi mwake mwadzaza.  
Iwo sadzachititsidwa manyazi  
pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.