Salimo 124
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. 
 
1 Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,  
anene tsono Israeli,   
2 akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,  
potiwukira anthuwo,   
3 iwo atatipsera mtima,  
akanatimeza amoyo;   
4 chigumula chikanatimiza,  
mtsinje ukanatikokolola,   
5 madzi a mkokomo  
akanatikokolola.   
   
 
6 Atamandike Yehova,  
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.   
7 Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame  
yokodwa mu msampha wa mlenje;  
msampha wathyoka,  
ndipo ife tapulumuka.   
8 Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova  
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.