Salimo 122
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. 
 
1 Ndinakondwera atandiwuza kuti,  
“Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”   
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata  
zako, Iwe Yerusalemu.   
   
 
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda  
umene uli wothithikana pamodzi.   
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko,  
mafuko a Yehova,  
umboni wa kwa Israeli,  
kuti atamande dzina la Yehova.   
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo,  
mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.   
   
 
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu:  
“Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.   
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako,  
ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”   
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga  
ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”   
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu,  
ndidzakufunira zabwino.