Salimo 113
Tamandani Yehova.
 
Mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
tamandani dzina la Yehova.
Yehova atamandidwe,
kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake,
dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
 
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse,
ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu,
Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
amene amawerama pansi kuyangʼana
miyamba ndi dziko lapansi?
 
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi
ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
amawakhazika pamodzi ndi mafumu,
pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake
monga mayi wa ana wosangalala.
 
Tamandani Yehova.