Salimo 112
1 Tamandani Yehova.  
   
 
Wodala munthu amene amaopa Yehova,  
amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.   
   
 
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;  
mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.   
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,  
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.   
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;  
wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.   
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,  
amene amachita ntchito yake mwachilungamo.   
   
 
6 Ndithu sadzagwedezeka;  
munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.   
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;  
mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.   
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;  
potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.   
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,  
chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;  
nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.   
   
 
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;  
adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.  
Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.