Salimo 111
1 Tamandani Yehova.  
   
 
Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse  
mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.   
   
 
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu;  
onse amene amakondwera nazo amazilingalira.   
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,  
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.   
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;  
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.   
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;  
amakumbukira pangano lake kwamuyaya.   
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,  
kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.   
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;  
malangizo ake onse ndi odalirika.   
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,  
ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.   
9 Iyeyo amawombola anthu ake;  
anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya  
dzina lake ndi loyera ndi loopsa.   
   
 
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;  
onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.  
Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.