Salimo 100
Salimo. Nyimbo yothokoza. 
 
1 Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.   
2 Mulambireni Yehova mosangalala;  
bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.   
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.  
Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake;  
ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.   
   
 
4 Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko  
ndi ku mabwalo ake ndi matamando;  
muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.   
5 Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya;  
kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.