Salimo 101
Salimo la Davide. 
 
1 Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama;  
kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.   
2 Ndidzatsata njira yolungama;  
nanga mudzabwera liti kwa ine?  
   
 
Ndidzayenda mʼnyumba mwanga  
ndi mtima wosalakwa.   
3 Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa  
pamaso panga.  
   
 
Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro;  
iwo sadzadziphatika kwa ine.   
4 Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine;  
ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.   
   
 
5 Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri  
ameneyo ndidzamuletsa;  
aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza,  
ameneyo sindidzamulekerera.   
   
 
6 Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko,  
kuti akhale pamodzi ndi ine;  
iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa  
adzanditumikira.   
   
 
7 Aliyense wochita chinyengo  
sadzakhala mʼnyumba mwanga.  
Aliyense woyankhula mwachinyengo  
sadzayima pamaso panga.   
   
 
8 Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu  
onse oyipa mʼdziko;  
ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa  
mu mzinda wa Yehova.