35
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza?
Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani,
ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
 
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu
pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone
mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani?
Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani?
Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo,
ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
 
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa;
akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga,
amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi
ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye
chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake;
Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti
Iye saona zimene zikuchitika.
Iye adzaweruza molungama ngati
inu mutamudikira
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango,
zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake,
mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”