Salimo 96
1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;  
Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.   
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;  
lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.   
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,  
ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.   
   
 
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;  
ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.   
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,  
koma Yehova analenga mayiko akumwamba.   
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,  
mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.   
   
 
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,  
perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.   
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;  
bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.   
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;  
njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.   
   
 
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”  
Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;  
Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.   
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;  
nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;   
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.  
Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;   
13 idzayimba pamaso pa Yehova,  
pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;  
adzaweruza dziko lonse mwachilungamo  
ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.