Salimo 70
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. 
 
1 Fulumirani Mulungu kundipulumutsa;  
Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.   
2 Iwo amene akufunafuna moyo wanga  
achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;  
onse amene akukhumba chiwonongeko changa  
abwezedwe mopanda ulemu.   
3 Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,”  
abwerere chifukwa cha manyazi awo.   
4 Koma onse amene akufunafuna Inu  
akondwere ndi kusangalala mwa Inu;  
iwo amene amakonda chipulumutso chanu  
nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”   
   
 
5 Koma ine ndine wosauka ndi wosowa;  
bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu.  
Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga;  
Inu Yehova musachedwe.