Salimo 43
1 Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;  
ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;  
mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.   
2 Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.  
Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?  
Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,  
woponderezedwa ndi mdani?   
3 Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu  
kuti zinditsogolere;  
mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,  
kumalo kumene inu mumakhala.   
4 Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,  
kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.  
Ndidzakutamandani ndi zeze,  
Inu Mulungu wanga.   
   
 
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?  
Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?  
Khulupirira Mulungu,  
pakuti ndidzamutamandabe Iye,  
Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.