Salimo 24
Salimo la Davide.
Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo,
dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja
ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
 
Ndani angakwere phiri la Yehova?
Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera,
amene sapereka moyo wake kwa fano
kapena kulumbira mwachinyengo.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova
ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova;
amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo.
Sela
 
Tukulani mitu yanu inu zipata;
tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,
kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?
Yehova Wamphamvuzonse,
Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
Tukulani mitu yanu, inu zipata;
tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,
kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?
Yehova Wamphamvuzonse,
Iye ndiye Mfumu yaulemerero.
Sela