Salimo 24
Salimo la Davide. 
 
1 Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo,  
dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;   
2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja  
ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.   
   
 
3 Ndani angakwere phiri la Yehova?  
Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?   
4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera,  
amene sapereka moyo wake kwa fano  
kapena kulumbira mwachinyengo.   
5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova  
ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.   
6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova;  
amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo.  
Sela
   
   
 
7 Tukulani mitu yanu inu zipata;  
tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,  
kuti Mfumu yaulemerero ilowe.   
8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?  
Yehova Wamphamvuzonse,  
Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.   
9 Tukulani mitu yanu, inu zipata;  
tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,  
kuti Mfumu yaulemerero ilowe.   
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?  
Yehova Wamphamvuzonse,  
Iye ndiye Mfumu yaulemerero.  
Sela