Salimo 22
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide.
Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?
Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?
Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,
usikunso, ndipo sindikhala chete.
 
Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;
ndinu matamando a Israeli.
Pa inu makolo athu anadalira;
iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.
Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
 
Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,
wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
Onse amene amandiona amandiseka;
amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
“Iyeyu amadalira Yehova,
musiyeni Yehovayo amulanditse.
Musiyeni Yehova amupulumutse
popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
 
Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.
Munachititsa kuti ndizikudalirani
ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;
kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11 Musakhale kutali ndi ine,
pakuti mavuto ali pafupi
ndipo palibe wina wondipulumutsa.
 
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira;
ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama,
yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi
ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.
Mtima wanga wasanduka phula;
wasungunuka mʼkati mwanga.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale,
ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;
mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
16 Agalu andizungulira;
gulu la anthu oyipa landizinga.
Alasa manja ndi mapazi anga.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse;
anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo
ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
 
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali;
Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga,
moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango;
pulumutseni ku nyanga za njati.
 
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga;
ndidzakutamandani mu msonkhano.
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni!
Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni!
Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza
kuvutika kwa wosautsidwayo;
Iye sanabise nkhope yake kwa iye.
Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
 
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira.
Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta;
iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda.
Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
27 Malekezero onse a dziko lapansi
adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye,
ndipo mabanja a mitundu ya anthu
adzawerama pamaso pake,
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova
ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
 
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira;
onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake;
iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye;
mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake
kwa anthu amene pano sanabadwe
pakuti Iye wachita zimenezi.