Salimo 20
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. 
 
1 Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso;  
dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.   
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika;  
akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.   
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse  
ndipo alandire nsembe zako zopsereza.  
Sela
   
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako  
ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.   
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana  
ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu,  
Yehova ayankhe zopempha zako zonse.   
   
 
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake;  
Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika  
ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.   
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo  
koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.   
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa,  
koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.   
   
 
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu!  
Tiyankheni pamene tikuyitanani!