Salimo 20
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso;
dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika;
akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Iye akumbukire nsembe zako zonse
ndipo alandire nsembe zako zopsereza.
Sela
Akupatse chokhumba cha mtima wako
ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana
ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu,
Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
 
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake;
Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika
ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo
koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa,
koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
 
Inu Yehova, pulumutsani mfumu!
Tiyankheni pamene tikuyitanani!