Salimo 16
Mikitamu ya Davide.
Ndisungeni Inu Mulungu,
pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
 
Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga;
popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko,
amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
Anthu amene amathamangira kwa milungu ina
mavuto awo adzachulukadi.
Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi
kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
 
Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa;
mwateteza kolimba gawo langa.
Malire a malo anga akhala pabwino;
ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
 
Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu;
ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.
Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja,
sindidzagwedezeka.
 
Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera;
thupi langanso lidzakhala pabwino,
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda,
simudzalola kuti woyera wanu avunde.
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo;
mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu,
ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.