Salimo 150
1 Tamandani Yehova.  
   
 
Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika;  
mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.   
2 Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu;  
mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.   
3 Mutamandeni poyimba malipenga,  
mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.   
4 Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina,  
mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.   
5 Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga,  
mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.   
   
 
6 Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova.  
   
 
Tamandani Yehova.