Salimo 145
Salimo la matamando la Davide.
Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;
ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku
ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
 
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;
ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;
Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,
ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,
ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,
ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
 
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Yehova ndi wabwino kwa onse;
amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;
oyera mtima adzakulemekezani.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu
ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu
ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,
ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.
 
Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse
ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa
ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu,
ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Mumatsekula dzanja lanu
ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
 
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,
ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,
onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;
amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda
koma adzawononga anthu onse oyipa.
 
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.
Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera
ku nthawi za nthawi.