Salimo 133
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. 
 
1 Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu  
pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!   
2 Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu,  
otsikira ku ndevu,  
ku ndevu za Aaroni,  
oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.   
3 Zili ngati mame a ku Heremoni  
otsikira pa Phiri la Ziyoni.  
Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso,  
ndiwo moyo wamuyaya.