Salimo 131
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide.
Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza,
maso anga siwonyada;
sinditengeteka mtima
ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
Koma moyo wanga ndawutontholetsa
ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa,
moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.
 
Yembekeza Yehova, iwe Israeli,
kuyambira tsopano mpaka muyaya.