Salimo 131
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide. 
 
1 Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza,  
maso anga siwonyada;  
sinditengeteka mtima  
ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.   
2 Koma moyo wanga ndawutontholetsa  
ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa,  
moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.   
   
 
3 Yembekeza Yehova, iwe Israeli,  
kuyambira tsopano mpaka muyaya.