Salimo 120
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,
ndipo Iye amandiyankha.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,
ndi kwa anthu achinyengo.
 
Kodi adzakuchitani chiyani,
ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,
ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
 
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,
kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati
pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Ine ndine munthu wamtendere;
koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.