Salimo 120
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. 
 
1 Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,  
ndipo Iye amandiyankha.   
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,  
ndi kwa anthu achinyengo.   
   
 
3 Kodi adzakuchitani chiyani,  
ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?   
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,  
ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.   
   
 
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,  
kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!   
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati  
pa iwo amene amadana ndi mtendere.   
7 Ine ndine munthu wamtendere;  
koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.