Masalimo   
BUKU LOYAMBA  
 1
Masalimo 1–41  
1 Wodala munthu  
amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,  
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,  
kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.   
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova  
ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.   
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,  
umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake  
ndipo masamba ake safota.  
Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.   
4 Sizitero ndi anthu oyipa!  
Iwo ali ngati mungu  
umene umawuluzidwa ndi mphepo.   
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,  
kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.   
   
 
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,  
koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.