4
Nzeru Iposa Zonse
Ananu, mverani malangizo a abambo anu;
tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino.
Choncho musasiye malangizo anga.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga;
mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti,
“Ugwiritse mawu anga pa mtima pako,
usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;
usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.
Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru.
Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza;
ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako;
idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
 
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena,
ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru.
Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana;
ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi.
Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa
kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo;
uzilambalala nʼkumangopita.
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa;
tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi
ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
 
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha
kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani;
iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
 
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena;
tchera khutu ku mawu anga.
21 Usayiwale malangizo angawa,
koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza
ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu
pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota;
ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo;
uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako
ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere;
usapite kumene kuli zoyipa.