3
1 Usiku wonse ndili pa bedi langa  
ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda;  
ndinamufunafuna koma osamupeza.   
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda,  
mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake;  
ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda.  
Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.   
3 Alonda anandipeza  
pamene ankayendera mzinda.  
“Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”   
4 Nditawapitirira pangʼono  
ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda.  
Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke  
mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,  
mʼchipinda cha amene anandibereka.   
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani  
pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:  
Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa  
mpaka pamene chifunire ichocho.   
   
 
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu  
ngati utsi watolotolo,  
wonunkhira mure ndi lubani,  
zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?   
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni,  
choperekezedwa ndi asilikali 60,  
anthu amphamvu a ku Israeli,   
8 onse atanyamula lupanga,  
onse odziwa bwino nkhondo,  
aliyense ali ndi lupanga pambali pake,  
kukonzekera zoopsa za usiku.   
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi;  
anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.   
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva,  
kumbuyo kwake kwa golide.  
Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo,  
anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi  
cha akazi a ku Yerusalemu.   
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni  
ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu,  
chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka  
pa tsiku la ukwati wake,  
tsiku limene mtima wake unasangalala.