3
Usiku wonse ndili pa bedi langa
ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda;
ndinamufunafuna koma osamupeza.
Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda,
mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake;
ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda.
Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
Alonda anandipeza
pamene ankayendera mzinda.
“Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
Nditawapitirira pangʼono
ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda.
Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke
mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,
mʼchipinda cha amene anandibereka.
Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani
pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:
Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa
mpaka pamene chifunire ichocho.
 
Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu
ngati utsi watolotolo,
wonunkhira mure ndi lubani,
zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni,
choperekezedwa ndi asilikali 60,
anthu amphamvu a ku Israeli,
onse atanyamula lupanga,
onse odziwa bwino nkhondo,
aliyense ali ndi lupanga pambali pake,
kukonzekera zoopsa za usiku.
Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi;
anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva,
kumbuyo kwake kwa golide.
Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo,
anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi
cha akazi a ku Yerusalemu.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni
ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu,
chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka
pa tsiku la ukwati wake,
tsiku limene mtima wake unasangalala.