Salimo 93
1 Yehova akulamulira, wavala ulemerero;  
Yehova wavala ulemerero ndipo wadzimangirira mphamvu,  
dziko lonse lakhazikika kolimba; silingasunthidwe.   
2 Mpando wanu waufumu unakhazikika kalekale;  
Inu ndinu wamuyaya.   
   
 
3 Nyanja zakweza Inu Yehova,  
nyanja zakweza mawu ake;  
nyanja zakweza mafunde ake ochita mkokomo.   
4 Yehova ndi wamphamvu kupambana mkokomo wa madzi ambiri,  
ndi wamphamvu kupambana mafunde a nyanja,  
Yehova mmwamba ndi wamphamvu.   
   
 
5 Malamulo anu Yehova ndi osasinthika;  
chiyero chimakongoletsa nyumba yanu  
mpaka muyaya.