Salimo 82
Salimo la Asafu.
Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;
Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
 
“Mudzateteza osalungama mpaka liti,
ndi kukondera anthu oyipa?
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;
mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;
apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
 
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.
Amayendayenda mu mdima;
maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
 
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,
nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
Koma mudzafa ngati anthu wamba;
mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
 
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,
pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.