Salimo 67
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.
Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,
achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,
chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
 
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,
pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo
ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
 
Nthaka yabereka zokolola zake;
tidalitseni Mulungu wathu.
Mulungu atidalitse
kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.