Salimo 30
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. 
 
1 Ndidzakukwezani Yehova,  
chifukwa mwanditulutsa kwakuya,  
ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.   
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo  
ndipo Inu munandichiritsa.   
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda,  
munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.   
   
 
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika;  
tamandani dzina lake loyera.   
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi  
koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse;  
utha kuchezera kulira usiku wonse,  
koma chimwemwe chimabwera mmawa.   
   
 
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati,  
“Sindidzagwedezekanso.”   
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima,  
munachititsa phiri langa kuyima chilili;  
koma pamene munabisa nkhope yanu,  
ndinataya mtima.   
   
 
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana;  
kwa Ambuye ndinapempha chifundo;   
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga  
ngati nditsikira ku dzenje?  
Kodi fumbi lidzakutamandani Inu?  
Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?   
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo;  
Yehova mukhale thandizo langa.”   
   
 
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina;  
munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,   
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete.  
Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.