Salimo 28
Salimo la Davide. 
 
1 Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;  
musakhale osamva kwa ine.  
Pakuti mukapitirira kukhala chete,  
ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.   
2 Imvani kupempha chifundo kwanga  
pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,  
pomwe ndikukweza manja anga  
kuloza ku malo anu oyeretsetsa.   
   
 
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,  
pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,  
amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo  
koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.   
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo  
ndi ntchito zawo zoyipa;  
abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita  
ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.   
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,  
ndi zimene manja ake anazichita,  
Iye adzawakhadzula  
ndipo sadzawathandizanso.   
   
 
6 Matamando apite kwa Yehova,  
popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.   
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;  
mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.  
Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe  
ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.   
   
 
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,  
linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.   
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;  
mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.