9
Za Nzeru ndi Uchitsiru 
 
1 Nzeru inamanga nyumba yake;  
inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.   
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake;  
inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.   
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake,  
kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,   
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!”  
Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,   
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa  
ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.   
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo;  
yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”   
   
 
7 Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo;  
aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.   
8 Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe;  
dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.   
9 Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru;  
ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.   
   
 
10 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru;  
kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.   
11 Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka,  
ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.   
12 Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa;  
ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.   
   
 
13 Uchitsiru ndi mkazi waphokoso,  
wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.   
14 Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake,  
pamalo aatali a mu mzinda,   
15 kuti aziyitana anthu ongodutsa,  
amene akunka nayenda njira zawo.   
16 Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,”  
ndipo kwa wopanda nzeru amati,   
17 “Madzi akuba ndiye amatsekemera;  
chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”   
18 Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko,  
ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya.