29
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri,
adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
 
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa,
koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
 
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake,
koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
 
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo,
koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
 
Munthu woshashalika mnzake,
akudziyalira ukonde mapazi ake.
 
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake,
koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
 
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka,
koma woyipa salabadira zimenezi.
 
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda,
koma anthu anzeru amaletsa ukali.
 
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru,
chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
 
10 Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro
koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
 
11 Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake,
koma munthu wanzeru amadzigwira.
 
12 Ngati wolamulira amvera zabodza,
akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
 
13 Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti:
Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
 
14 Ngati mfumu iweruza osauka moyenera,
mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
 
15 Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru
koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
 
16 Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka,
koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
 
17 Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere
ndi kusangalatsa mtima wako.
 
18 Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo;
koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
 
19 Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi;
ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
 
20 Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo
kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
 
21 Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana,
potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
 
22 Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano,
ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
 
23 Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa,
koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
 
24 Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe;
amalumbira koma osawulula kanthu.
 
25 Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha,
koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
 
26 Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima,
koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
 
27 Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo;
koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.