13
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake,
koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
 
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake,
koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
 
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,
koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
 
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu,
koma munthu wakhama adzalemera.
 
Munthu wolungama amadana ndi zabodza,
koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
 
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro,
koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
 
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse;
munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
 
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake,
koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
 
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa,
koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
 
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano,
koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
 
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono
koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
 
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima,
koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
 
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka,
koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
 
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo;
amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
 
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu,
koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
 
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru,
koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
 
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto,
koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
 
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa,
koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
 
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima,
koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
 
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru;
koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
 
21 Choyipa chitsata mwini,
koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
 
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa,
koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
 
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri,
koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
 
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda,
koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
 
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta,
koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.