11
Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa,
koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
 
Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi,
koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
 
Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera,
koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
 
Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu,
koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
 
Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo,
koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
 
Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa,
koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
 
Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso.
Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
 
Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto,
koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
 
Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake,
koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
 
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera,
ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
 
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima,
koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
 
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru,
koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
 
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi;
koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
 
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa;
koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
 
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto,
koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
 
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu,
koma amuna ankhanza amangopata chuma.
 
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino
koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
 
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu,
koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
 
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo,
koma wothamangira zoyipa adzafa.
 
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota
koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
 
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa,
koma anthu olungama adzapulumuka.
 
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba,
ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
 
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha,
koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
 
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe;
wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
 
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera;
iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
 
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya,
koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
 
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo,
koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
 
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota,
koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
 
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto,
ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
 
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo,
ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
 
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi,
kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!