35
Chimwemwe cha Opulumutsidwa 
 
1 Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala;  
dziko lowuma lidzakondwa  
ndi kuchita maluwa.  
2 Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka  
lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe.  
Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni,  
maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni.  
   
 
Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova,  
ukulu wa Mulungu wathu.   
3 Limbitsani manja ofowoka,  
limbitsani mawondo agwedegwede;   
4 nenani kwa a mitima yamantha kuti;  
“Limbani mtima, musachite mantha;  
Mulungu wanu akubwera,  
akubwera kudzalipsira;  
ndi kudzabwezera chilango adani anu;  
akubwera kudzakupulumutsani.”   
   
 
5 Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso  
ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.   
6 Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala,  
ndipo osayankhula adzayimba mokondwera.  
Akasupe adzatumphuka mʼchipululu  
ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,   
7 mchenga wotentha udzasanduka dziwe,  
nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe.  
Pamene panali mbuto ya ankhandwe  
padzamera udzu ndi bango.   
   
 
8 Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu;  
ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika.  
Anthu odetsedwa  
sadzayendamo mʼmenemo;  
zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.   
9 Kumeneko sikudzakhala mkango,  
ngakhale nyama yolusa sidzafikako;  
sidzapezeka konse kumeneko.  
Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.   
10 Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera.  
Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba;  
kumeneko adzakondwa mpaka muyaya.  
Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe,  
ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.