15
Za Kulangidwa kwa Mowabu 
 
1 Uthenga wonena za Mowabu:  
Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,  
wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.  
Mzinda wa Kiri wawonongedwa,  
wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.   
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,  
akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;  
anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.  
Mutu uliwonse wametedwa mpala,  
ndipo ndevu zonse zametedwa.   
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli;  
pa madenga ndi mʼmabwalo  
aliyense akulira mofuwula,  
misozi ili pupupu.   
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,  
mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.  
Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,  
ndipo ataya mtima.   
   
 
5 Inenso ndikulirira Mowabu;  
chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari  
ndi Egilati-Selisiya  
akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,  
Akulira mosweka mtima  
pa njira yopita ku Horonaimu;  
akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.   
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa  
ndipo udzu wauma;  
zomera zawonongeka  
ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.   
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,  
achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.   
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;  
kulira kwawo kosweka mtima kukumveka  
mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.   
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,  
komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,  
mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu  
ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.