12
Nyimbo za Mayamiko 
 
1 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:  
“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;  
chifukwa ngakhale munandipsera mtima,  
mkwiyo wanu wachoka,  
ndipo mwanditonthoza.   
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;  
ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.  
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;  
Iye wakhala chipulumutso changa.”   
3 Mudzakondwera popeza Yehova  
ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.   
4 Tsiku limenelo mudzati:  
“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;  
mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,  
ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.   
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;  
zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.   
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;  
pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”